Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 1/13 tsamba 4
  • Zitsanzo za Ulaliki

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zitsanzo za Ulaliki
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Nkhani Yofanana
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2012
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
km 1/13 tsamba 4

Zitsanzo za Ulaliki

Zimene Munganene Poyambitsa Maphunziro a Baibulo Loweruka Loyambirira M’mwezi wa February

“Anthu ambiri amaganiza kuti Mdyerekezi ndi amene akuchititsa zinthu zonse zoipa m’dzikoli. Komabe, iwo amadzifunsa kuti: ‘Kodi Mdyerekezi anachokera kuti? Kodi iye analengedwa ndi Mulungu?’ Kodi inuyo mukuganiza bwanji? [Yembekezani ayankhe.] Taonani zimene zili apazi.” Musonyezeni nkhani imene ili patsamba lomaliza la Nsanja ya Olonda ya February 1, 2013, ndipo werengani ndi kukambirana ndime yoyamba pamodzi ndi lemba lake. Mugawireni magaziniyo ndipo konzani zoti mudzabwerenso kuti mudzakambirane funso lotsatira.

Nsanja ya Olonda February 1

“Tikufuna timve maganizo anu pa nkhani yokhudza munthu wina wake amene amalemekezedwa kwambiri ndi Akhristu, Ayuda ndiponso Asilamu. Munthu ameneyu ndi Mose. Kodi n’chiyani chimene chimabwera m’maganizo anu mukamva dzina lake? [Yembekezani ayankhe.] N’zochititsa chidwi kuona zimene Baibulo limanena zokhudza Mose ngakhale kuti analakwitsapo zinthu zina. [Werengani Deuteronomo 34:10-12.] Magazini iyi ikufotokoza atatu mwa makhalidwe ake abwino amene tingawatsanzire.”

Galamukani! February

“Masiku ano, anthu ambiri akusamukira kumayiko ena pothawa mavuto m’mayiko awo. Kodi mukuganiza kuti anthu amenewa nthawi zonse amapezadi zimene akufuna? [Yembekezani ayankhe.] Anthu sanayambe lero kusamukira m’mayiko ena. Taonani chitsanzo ichi cha anthu ena amene anasamuka kwawo, chomwe chikupezeka m’buku loyambirira m’Baibulo. [Werengani Genesis 46:5, 6.] Magazini iyi ikuyankha mafunso awa.” Sonyezani mwininyumba mafunso amene ali kumapeto kwa tsamba 6.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena