Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb16 February tsamba 8
  • Itanirani Anthu Onse M’gawo Lanu ku Chikumbutso

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Itanirani Anthu Onse M’gawo Lanu ku Chikumbutso
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • ZIMENE MUNGACHITE
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Kugawira Timapepala Toitanira Anthu ku Chikumbutso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Yehova Amadalitsa Khama Lathu Loyesetsa Kuti Tipezeke pa Chikumbutso
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
  • Ntchito Yapadera Yoitanira Anthu ku Chikumbutso Idzayamba pa March 17
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2012
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
mwb16 February tsamba 8

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Itanirani Anthu Onse M’gawo Lanu ku Chikumbutso

Losindikizidwa
Kapepala Koitanira Anthu ku Mwambo Wokumbukira Imfa ya Khristu mu 2016

Ntchito yapadera yoitanira anthu ku Chikumbutso iyamba pa February 27. Tikufunitsitsa kuitanira anthu ambiri kumwambo wokumbukira imfa ya Khristu umenewu. Komanso tiyenera kuonetsetsa anthu amene asonyeza chidwi n’kuwathandiza.

ZIMENE MUNGACHITE

PEREKANI KAPEPALA

“Tikupereka kapepala aka kwa anthu powaitanira kumwambo wofunika kwambiri. Pa March 23, anthu ambiri padziko lonse adzasonkhana kuti akumbukire imfa ya Yesu Khristu. Pamwambowo adzamvetsera nkhani yofotokoza mmene imfa ya Yesu imatithandizira. Zonsezi zidzachitika popanda kuyendetsa mbale ya zopereka. Malo komanso nthawi imene mwambowu udzachitike, talemba papepalali. Muyesetse kudzabwera.”

Ngati munthuyo wasonyeza chidwi chitani izi:

  • PEREKANI NSANJA YA OLONDA

    Muuzeni nkhani imene mudzakambirane ulendo wotsatira.

  • ONETSANI VIDIYO YA CHIKUMBUTSO

    Muuzeni zimene mudzaphunzire ulendo wotsatira.

Mukadzakumananso mukhoza kudzachita zotsatirazi:

  • ONETSANI VIDIYO YAKUTI N’CHIFUKWA CHIYANI TIYENERA KUPHUNZIRA BAIBULO?

    Kenako perekani buku kapena kabuku koti muziphunzira naye.

  • PEREKANI BUKU LAKUTI KODI BAIBULO LIMAPHUNZITSA CHIYANI KWENIKWENI?

    Kambiranani mfundo zokhudza Chikumbutso patsamba 206-208. Kenako perekani bukulo.

  • PEREKANI KABUKU KAKUTI MVERANI MULUNGU

    Kambiranani tsamba 18-19 kuti aone mmene imfa ya Khristu imatithandizira.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena