Akuitanira anthu kumisonkhano ku Cook Islands
Zitsanzo za Ulaliki
NSANJA YA OLONDA
Funso: Kodi angelo alipodi?
Lemba: Sal. 103:20
Perekani Magaziniyo: Nsanja ya Olonda iyi ikufotokoza zimene Baibulo limanena zokhudza angelo ndiponso mmene amatithandizira masiku ano.
KUPHUNZITSA CHOONADI
Funso: Kodi mumaona kuti sayansi imatsutsana ndi Baibulo?
Lemba: Yes. 40:22
Zoona Zake: Zimene Baibulo limanena pa nkhani za sayansi n’zolondola.
KAPEPALA KOITANIRA ANTHU KUMISONKHANO (inv)
Munganene Kuti: Ndikukuitanirani kumisonkhano yathu kuti mudzamvetsere nkhani yochokera m’Baibulo. Idzakambidwa ku Nyumba ya Ufumu omwe ndi malo athu olambirira. [Perekani kapepalako ndipo musonyezeni nthawi komanso malo a misonkhanoyo. Muuzeninso mutu wa nkhani ya mlungu umenewo.]
Funso: Kodi munayamba mwapitapo ku Nyumba ya Ufumu? [Ngati n’zotheka muonetseni vidiyo yakuti Kodi pa Nyumba ya Ufumu Pamachitika Zotani?]
LEMBANI ULALIKI WANUWANU
Potengera zitsanzozi, konzani njira imene mungagwiritse ntchito.