1 Mbiri
8 Benjamini+ anabereka Bela+ mwana wake woyamba, wachiwiri anali Asibeli,+ wachitatu anali Ahara,+ 2 wachinayi anali Noha,+ ndipo wachisanu anali Rafa. 3 Ana a Bela anali Adara, Gera,+ Abihudi, 4 Abisuwa, Namani, Ahowa, 5 Gera, Sefufani,+ ndi Huramu.+ 6 Panalinso ana a Ehudi amene anali atsogoleri a nyumba za makolo a anthu okhala ku Geba.+ Iwowa anagwira anthu ndi kuwatengera ku Manahati. 7 Atsogoleriwo anali Namani, Ahiya, ndi Gera. Gera ndiye anatengera anthuwo ku ukapolo, ndipo iye anabereka Uziza ndi Ahihudi. 8 Saharaimu anabereka ana m’dziko+ la Mowabu atathamangitsako Amowabu. Akazi ake anali Husimu ndi Baara. 9 Kwa Hodesi mkazi wake, anabereka Yobabi, Zibia, Mesa, Malikamu, 10 Yeuzi, Sakiya, ndi Mirima. Amenewa anali ana ake, atsogoleri a nyumba za makolo awo.
11 Kwa Husimu anabereka Abitubu ndi Elipaala. 12 Ana a Elipaala anali Ebere, Misamu, ndi Semedi. Semedi ndiye anamanga mzinda wa Ono+ ndiponso mzinda wa Lodi,+ ndi midzi yake yozungulira. 13 Elipaala anaberekanso Beriya ndi Sema. Amenewa anali atsogoleri a nyumba za makolo a anthu okhala ku Aijaloni.+ Iwo ndiwo anathamangitsa anthu a ku Gati. 14 Panalinso Ahiyo, Sasaki, Yeremoti, 15 Zebadiya, Aradi, Ederi, 16 Mikayeli, Isipa, ndi Yoha. Amenewa anali ana a Beriya.+ 17 Zebadiya, Mesulamu, Hiziki, Hiberi, 18 Isimerai, Iziliya, ndi Yobabi anali ana a Elipaala. 19 Yakimu, Zikiri, Zabidi, 20 Elianai, Ziletai, Elieli, 21 Adaya, Beraya, ndi Simirati, anali ana a Simeyi.+ 22 Isipani, Ebere, Elieli, 23 Abidoni, Zikiri, Hanani, 24 Hananiya, Elamu, Antotiya, 25 Ifideya, ndi Penueli, anali ana a Sasaki. 26 Samuserai, Sehariya, Ataliya, 27 Yaaresiya, Eliya, ndi Zikiri, anali ana a Yerohamu. 28 Amenewa anali atsogoleri a nyumba za makolo awo motsatira mzere wa mabanja awo. Iwowa ndi amene anali kukhala ku Yerusalemu.+
29 Yeyeli bambo wa Gibeoni+ anali kukhala ku Gibeoni, ndipo dzina la mkazi wake linali Maaka.+ 30 Mwana wake woyamba anali Abidoni. Anaberekanso Zuri, Kisi, Baala, Nadabu,+ 31 Gedori, Ahiyo, ndi Zekeri.+ 32 Mikiloti anabereka Simeya.+ Amenewa ndiwo anali kukhala ku Yerusalemu pamodzi ndi abale awo ena, moyang’anizana ndi abale awo.
33 Nera+ anabereka Kisi,+ Kisi anabereka Sauli,+ Sauli anabereka Yonatani,+ Malikisuwa,+ Abinadabu,+ ndi Esibaala.+ 34 Mwana wa Yonatani anali Meribi-baala,+ ndipo Meribi-baala anabereka Mika.+ 35 Ana a Mika anali Pitoni, Meleki, Tarea,+ ndi Ahazi. 36 Ahazi anabereka Yehoada. Yehoada anabereka Alemeti, Azimaveti, ndi Zimiri. Zimiri anabereka Moza. 37 Moza anabereka Bineya, Bineya anabereka Rafa,+ Rafa anabereka Eleasa, ndipo Eleasa anabereka Azeli. 38 Azeli anali ndi ana 6. Mayina awo anali, Azirikamu, Bokeru, Isimaeli, Seariya, Obadiya, ndi Hanani. Onsewa anali ana a Azeli. 39 Ana a m’bale wake Ezeki anali awa: woyamba Ulamu, wachiwiri Yeusi, wachitatu Elifeleti. 40 Ana a Ulamu anali amuna amphamvu ndi olimba mtima,+ amuna odziwa kupinda uta.+ Iwo anali ndi ana ambiri+ ndiponso zidzukulu zambiri. Onse analipo 150. Onsewa anali ana a Benjamini.