Numeri
36 Atsogoleri a mabanja a ana a Giliyadi mwana wa Makiri,+ mwana wa Manase, ochokera kumabanja a ana a Yosefe, anafika ndi kulankhula ndi Mose ndi akalonga omwe anali atsogoleri a ana a Isiraeli. 2 Iwo anati: “Paja Yehova anakulamulani inu mbuyathu, kuti mugawire dzikoli ana a Isiraeli monga cholowa chawo, mwa kuchita maere.+ Yehova anakulamulaninso kuti cholowa cha m’bale wathu Tselofekadi muchipereke kwa ana ake aakazi.+ 3 Tsopano ana aakaziwa akadzakwatiwa ndi amuna a mafuko ena a ana a Isiraeli, ndiye kuti cholowa chawo chidzachotsedwa ku cholowa cha makolo athu, ndipo chidzawonjezedwa ku cholowa cha fuko limene aliyense adzakwatiweko. Zikadzatero ndiye kuti cholowa chathu cha malo chidzachepa.+ 4 Chaka cha Ufulu+ cha ana a Isiraeli chikadzafika, cholowa cha akaziwa chidzachotsedwa ku cholowa cha fuko la makolo athu, ndipo chidzawonjezedwa ku cholowa cha fuko limene aliyense wa iwo adzakwatiweko ndipo chidzakhala cha fukolo mpaka kalekale.”
5 Pamenepo Mose anauza ana a Isiraeli zimene Yehova anamuuza, kuti: “Fuko la ana a Yosefe likunena zoona. 6 Zimene Yehova walamula zokhudza ana aakazi a Tselofekadi+ n’zakuti, ‘Iwo angakwatiwe ndi aliyense amene wawakomera m’maso. Koma akwatiwe ndi amuna a fuko la makolo awo okha.+ 7 Cholowa cha ana a Isiraeli chisachoke ku fuko lina kupita ku fuko lina. Aliyense wa ana a Isiraeli ayenera kusunga cholowa cha fuko la makolo ake. 8 Choncho, mwana wamkazi aliyense amene walandira nawo cholowa pakati pa mafuko a ana a Isiraeli, azikwatiwa ndi mwamuna wa m’banja la fuko la bambo ake,+ kuti aliyense wa ana a Isiraeli azilandira cholowa chochokera kwa makolo ake. 9 Cholowa chilichonse chisachoke ku fuko lina kupita ku fuko lina. Fuko lililonse la ana a Isiraeli lizisunga cholowa chake.’”
10 Ana aakazi a Tselofekadi amenewo anachitadi zimene Yehova analamula Mose.+ 11 Chotero, Mala, Tiriza, Hogila, Milika, ndi Nowa, ana aakazi a Tselofekadi,+ anakwatiwa ndi ana a abale* a bambo awo. 12 Anakwatiwa ku mabanja a ana a Manase mwana wa Yosefe, kuti cholowa chawo chisachoke ku fuko la banja la bambo awo.
13 Amenewa ndiwo malamulo+ ndi zigamulo za Yehova, zimene anapereka kwa ana a Isiraeli kudzera kwa Mose ku Yeriko, m’chipululu cha Mowabu, pafupi ndi mtsinje wa Yorodano.+