Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Genesis 13:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Choncho, Loti anakweza maso ake n’kuona Chigawo* chonse cha Yorodano+ mpaka kukafika ku Zowari,+ ndipo anaona kuti chinali chigawo chobiriwira bwino. Chinali chobiriwira bwino kwambiri ngati mmene unalili munda wa Yehova+ komanso ngati mmene linalili dziko la Iguputo. Pa nthawiyi n’kuti Yehova asanawononge Sodomu ndi Gomora.

  • Salimo 107:34
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 Nthaka yobala zipatso amaisandutsa dziko lamchere,+

      Chifukwa cha kuipa kwa anthu okhala mmenemo.

  • Yeremiya 49:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Monga mmene Sodomu ndi Gomora pamodzi ndi midzi yapafupi inawonongedwera,+ Edomu adzawonongedwanso moti palibe munthu amene adzakhalanso m’dzikolo. Mwana wa munthu sadzakhalanso mmenemo ngati mlendo,”+ watero Yehova.

  • Zefaniya 2:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Yehova wa makamu, Mulungu wa Isiraeli wanena kuti: “Pali ine Mulungu wamoyo,+ Mowabu adzakhala ndendende ngati Sodomu,+ ndipo ana a Amoni+ adzakhala ngati Gomora, malo odzaza zomera zoyabwa ndiponso mchere ndiponso malo abwinja mpaka kalekale.*+ Otsala mwa anthu anga adzafunkha zinthu zawo, ndipo otsala a mtundu wa anthu anga adzawagwira ukapolo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena