Genesis 12:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Ine ndidzatulutsa mtundu waukulu mwa iwe. Ndidzakudalitsa ndi kukuza dzina lako, ndipo iwe ukhale dalitso+ kwa ena. Genesis 15:5 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 5 Kenako anamutengera panja, n’kumuuza kuti: “Kweza maso ako kumwamba, uwerenge nyenyezizo ngati ungathe kuziwerenga.”+ Ndipo anamuuzanso kuti: “Umu ndi mmene mbewu yako idzakhalire.”+ Genesis 46:3 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 3 Mulungu anapitiriza kuti: “Ine ndine Mulungu woona,+ Mulungu wa bambo ako.+ Usaope kupita ku Iguputo, chifukwa kumeneko ndidzakukuza kukhala mtundu waukulu.+ Ekisodo 1:7 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 7 Ana a Isiraeli anaberekana ndipo anachuluka m’dzikomo. Iwo anapitiriza kuchulukana ndi kukhala amphamvu koposa, moti anadzaza m’dzikomo.+ Ekisodo 38:26 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 26 Mwamuna aliyense amene anawerengedwa, kuyambira wa zaka 20 kupita m’tsogolo,+ anapereka hafu ya sekeli lolingana ndi hafu ya sekeli la kumalo oyera. Owerengedwa onse anakwana 603,550.+ Numeri 2:32 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 32 Amenewa ndiwo anali olembedwa mayina a ana a Isiraeli, malinga ndi nyumba ya makolo awo. Asilikali onse olembedwa mayina m’misasa yonse, analipo 603,550.+ Numeri 11:21 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 21 Koma Mose anati: “Amuna amene ndikuyenda nawo akukwana 600,000,+ koma inuyo mukunena kuti, ‘Nyamayo ndiwapatsa, ndipo adzaidya kwa mwezi wonse wathunthu.’
2 Ine ndidzatulutsa mtundu waukulu mwa iwe. Ndidzakudalitsa ndi kukuza dzina lako, ndipo iwe ukhale dalitso+ kwa ena.
5 Kenako anamutengera panja, n’kumuuza kuti: “Kweza maso ako kumwamba, uwerenge nyenyezizo ngati ungathe kuziwerenga.”+ Ndipo anamuuzanso kuti: “Umu ndi mmene mbewu yako idzakhalire.”+
3 Mulungu anapitiriza kuti: “Ine ndine Mulungu woona,+ Mulungu wa bambo ako.+ Usaope kupita ku Iguputo, chifukwa kumeneko ndidzakukuza kukhala mtundu waukulu.+
7 Ana a Isiraeli anaberekana ndipo anachuluka m’dzikomo. Iwo anapitiriza kuchulukana ndi kukhala amphamvu koposa, moti anadzaza m’dzikomo.+
26 Mwamuna aliyense amene anawerengedwa, kuyambira wa zaka 20 kupita m’tsogolo,+ anapereka hafu ya sekeli lolingana ndi hafu ya sekeli la kumalo oyera. Owerengedwa onse anakwana 603,550.+
32 Amenewa ndiwo anali olembedwa mayina a ana a Isiraeli, malinga ndi nyumba ya makolo awo. Asilikali onse olembedwa mayina m’misasa yonse, analipo 603,550.+
21 Koma Mose anati: “Amuna amene ndikuyenda nawo akukwana 600,000,+ koma inuyo mukunena kuti, ‘Nyamayo ndiwapatsa, ndipo adzaidya kwa mwezi wonse wathunthu.’