Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Samueli 11:25
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 25 Pamenepo Davide anauza mthengayo kuti: “Ukamuuze Yowabu kuti, ‘Usavutike mtima chifukwa cha nkhani imeneyi, pakuti lupanga lingakanthe+ wina aliyense. Inuyo menyani nkhondo mwamphamvu ndi mzindawo ndipo muugonjetse.’+ Choncho, ukamulimbikitse Yowabu.”

  • Yesaya 1:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Koma mukakana+ n’kupanduka, mudzawonongedwa ndi lupanga, chifukwa pakamwa pa Yehova m’pamene panena zimenezi.”+

  • Yeremiya 2:30
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 30 Ndalanga ana anu aamuna koma sizinathandize.+ Iwo sanamve chilango* changa.+ Lupanga lanu lapha aneneri anu, ngati mkango umene ukupha anthu ambiri.+

  • Yeremiya 12:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Anthu ofunkha adutsa m’njira zonse zodutsidwadutsidwa za m’chipululu. Lupanga la Yehova likuwononga anthu kuchokera kumalekezero a dziko kukafika kumalekezero ena a dziko.+ Palibe mtendere kwa munthu aliyense.

  • Yeremiya 46:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 “Limeneli ndi tsiku la Yehova wa makamu, Ambuye Wamkulu Koposa ndipo ndi tsiku lobwezera chilango kwa adani ake.+ Lupanga lidzadya adaniwo ndi kukhuta ndipo lidzamwa magazi awo kufikira litathetsa ludzu lake. Lidzatero pakuti Yehova wa makamu, Ambuye Wamkulu Koposa,+ ali ndi nsembe imene akufuna kupereka+ m’dziko la kumpoto, m’mphepete mwa mtsinje wa Firate.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena