-
Yesaya 34:6Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
6 Yehova ali ndi lupanga. Lupangalo lidzakhala magazi okhaokha+ ndipo lidzaterera ndi mafuta. Lidzadzaza magazi a nkhosa zamphongo zing’onozing’ono ndi a mbuzi zamphongo. Lidzaterera ndi mafuta+ a impso za nkhosa zamphongo, pakuti Yehova adzapereka nsembe ku Bozira ndipo adzapha nyama zambiri m’dziko la Edomu.+
-
-
Ezekieli 39:17Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
17 “Koma kwa iwe mwana wa munthu, Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti, ‘Uza mbalame zamitundumitundu ndi zilombo zonse zakutchire+ kuti: “Sonkhanani mubwere kuno. Sonkhanani pamodzi kuzungulira nsembe yanga imene ndikukuperekerani. Imeneyi ndi nsembe yaikulu m’mapiri a ku Isiraeli.+ Mukabwera mudzadya nyama ndi kumwa magazi.+
-