-
Yesaya 34:6Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
6 Yehova ali ndi lupanga. Lupangalo lidzakhala magazi okhaokha+ ndipo lidzaterera ndi mafuta. Lidzadzaza magazi a nkhosa zamphongo zing’onozing’ono ndi a mbuzi zamphongo. Lidzaterera ndi mafuta+ a impso za nkhosa zamphongo, pakuti Yehova adzapereka nsembe ku Bozira ndipo adzapha nyama zambiri m’dziko la Edomu.+
-
-
Yeremiya 46:10Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
10 “Limeneli ndi tsiku la Yehova wa makamu, Ambuye Wamkulu Koposa ndipo ndi tsiku lobwezera chilango kwa adani ake.+ Lupanga lidzadya adaniwo ndi kukhuta ndipo lidzamwa magazi awo kufikira litathetsa ludzu lake. Lidzatero pakuti Yehova wa makamu, Ambuye Wamkulu Koposa,+ ali ndi nsembe imene akufuna kupereka+ m’dziko la kumpoto, m’mphepete mwa mtsinje wa Firate.+
-