Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mbiri 36:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Koma iwo ankangonyogodola+ amithenga a Mulungu woona, kunyoza mawu ake+ ndi kuseka+ aneneri ake, mpaka kufika poti panalibenso chiyembekezo choti angathe kuchiritsidwa.+ Kenako mkwiyo+ wa Yehova unawagwera.

  • Nehemiya 9:26
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 “Koma iwo anakhala osamvera+ ndipo anakupandukirani.+ Anapitiriza kufulatira chilamulo chanu,+ ndipo anapha aneneri anu+ amene anali kuwalimbikitsa kuti abwerere kwa inu.+ Iwo anapitiriza kuchita zinthu zikuluzikulu zosakulemekezani.+

  • Mateyu 21:35
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 35 Koma alimi aja anagwira akapolo ake aja ndipo mmodzi anam’menya, wina anamupha, wina anam’ponya miyala.+

  • Mateyu 23:34
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 Pa chifukwa chimenechi, tsopano ndikukutumizirani+ aneneri, anthu anzeru ndi aphunzitsi.+ Ena a iwo mudzawapha+ ndi kuwapachika, ndipo ena mudzawakwapula+ m’masunagoge mwanu ndi kuwazunza mumzinda ndi mzinda,

  • Machitidwe 7:52
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 52 Ndi mneneri uti amene makolo anuwo sanamuzunze?+ Inde, iwo anapha+ amene analengezeratu za kubwera kwa Wolungamayo,+ amene inuyo munamupereka ndi kumupha,+

  • 1 Atesalonika 2:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 amene anapha ngakhale Ambuye Yesu+ ndi aneneri+ ndi kuzunzanso ifeyo.+ Ndipo iwo sakukondweretsa Mulungu, koma akutsekereza zinthu zopindulitsa anthu onse.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena