-
1 Samueli 26:19Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
19 Tsopano mbuyanga mfumu, mvetserani mawu a mtumiki wanu: Ngati Yehova ndiye wakutumani kuti mundiukire, iye alandire nsembe yanga yambewu.+ Koma ngati ndi ana a anthu,+ atembereredwe pamaso pa Yehova,+ chifukwa andipitikitsa ndi kundichotsa lero kuti ndisamve kuti ndili pafupi ndi cholowa cha Yehova,+ mwa kundiuza kuti, ‘Pita ukatumikire milungu ina!’+
-
-
1 Mbiri 5:26Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
26 Choncho, Mulungu wa Isiraeli analimbikitsa mtima+ wa Puli+ mfumu ya Asuri,+ ndithu analimbikitsa mtima wa Tigilati-pilenesere+ mfumu ya Asuri, moti anatenga+ Arubeni, Agadi, ndi hafu ya fuko la Manase n’kuwapititsa ku Hala,+ ku Habori, ku Hara, ndi kumtsinje wa Gozani, ndipo akukhalabe kumeneko mpaka lero.
-