59 Yehova adzakulitsa kwambiri miliri yako ndi miliri ya ana ako. Miliri imeneyo idzakhala yaikulu kwambiri ndi yokhalitsa,+ ndipo udzagwidwa ndi matenda onyansa ndi okhalitsa.+
17 Ine ndinanena mumtima mwanga+ kuti: “Mulungu woona adzaweruza munthu wolungama ndi munthu woipa,+ pakuti iye ali ndi nthawi yochitira chinthu chilichonse ndiponso yokhudza ntchito iliyonse.”+