3 Mitunduyo ndi olamulira asanu ogwirizana+ a Afilisiti,+ Akanani onse,+ ngakhalenso Asidoni+ ndi Ahivi+ okhala m’phiri la Lebanoni,+ kuchokera kuphiri la Baala-herimoni+ mpaka kumalire a dera la Hamati.+
19 Anamanganso mizinda yake yonse yosungirako zinthu,+ mizinda yosungirako magaleta,+ mizinda ya amuna okwera pamahatchi, ndiponso zilizonse zimene iye anakonda+ kumanga ku Yerusalemu, ku Lebanoni, ndi m’dziko lonse limene ankalamulira.