17 ‘Ndithudi, maso ako ndi mtima wako sizikulakalaka china chilichonse koma phindu lachinyengo,+ anthu osalakwa kuti ukhetse magazi awo+ komanso kuba mwachinyengo ndi kulanda.’
9 Tamverani izi inu atsogoleri a nyumba ya Yakobo komanso inu olamulira a nyumba ya Isiraeli,+ amene mukuipidwa ndi chilungamo ndiponso amene mukupotoza chilichonse chowongoka.+