8 “Tsopano anthu inu mukuganiza zolimbana ndi ufumu wa Yehova umene uli m’manja mwa ana a Davide,+ popeza ndinu khamu lalikulu+ ndipo muli ndi ana a ng’ombe agolide amene Yerobowamu anakupangirani kuti akhale milungu yanu.+
12 Taonani, ife patsogolo pathu pali Mulungu woona+ ndi ansembe ake,+ ndi malipenga+ otiitanira ku nkhondo yomenyana nanu. Inu ana a Isiraeli, musamenyane ndi Yehova Mulungu wa makolo anu,+ chifukwa simupambana.”+