Oweruza 9:13 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 13 Poyankha mtengo wa mpesawo unati, ‘Kodi ndisiye vinyo wanga watsopano amene amasangalatsa Mulungu ndi anthu,+ n’kupita kuti ndizikagwedezeka pamwamba pa mitengo ina?’ 2 Samueli 13:28 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 28 Kenako Abisalomu analamula omutumikira kuti: “Muonetsetse chonde kuti Aminoni akangosangalala mumtima mwake ndi vinyo,+ ine n’kukuuzani kuti, ‘Mukantheni Aminoni!’ pamenepo mumuphe. Musaope.+ Kodi si ndine amene ndakulamulani? Chitani zinthu mwamphamvu ndipo khalani olimba mtima.” Esitere 1:10 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 10 Pa tsiku la 7, pamene mtima wa mfumu unali kukondwera ndi vinyo,+ mfumu inauza Mehumani, Bizita, Haribona,+ Bigita, Abagata, Zetara ndi Karikasi, nduna 7 za panyumba ya mfumu zimene zinali kutumikira+ Mfumu Ahasiwero, Miyambo 31:6 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 6 Anthu inu, perekani chakumwa choledzeretsa kwa munthu amene watsala pang’ono kuwonongedwa+ ndi vinyo kwa anthu amene mtima wawo ukuwawa.+ Mlaliki 2:3 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 3 Ndinafufuza ndi mtima wanga wonse kuti ndidziwe uchitsiru posangalatsa thupi langa ndi vinyo,+ pamene ndinali kutsogolera mtima wanga ndi nzeru.+ Ndinachita zimenezi kuti ndione ubwino umene ana a anthu amapeza pa zimene amachita padziko lapansi pano masiku onse a moyo wawo.+ Mlaliki 9:7 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 7 Pita ukadye chakudya chako mokondwera ndi kumwa vinyo wako ndi mtima wosangalala,+ chifukwa Mulungu woona wakondwera kale ndi ntchito zako.+ Mlaliki 10:19 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 19 Chakudya chimachititsa antchito kuseka, ndipo vinyo amachititsa moyo kusangalala,+ koma ndalama zimathandiza pa zinthu zonse.+
13 Poyankha mtengo wa mpesawo unati, ‘Kodi ndisiye vinyo wanga watsopano amene amasangalatsa Mulungu ndi anthu,+ n’kupita kuti ndizikagwedezeka pamwamba pa mitengo ina?’
28 Kenako Abisalomu analamula omutumikira kuti: “Muonetsetse chonde kuti Aminoni akangosangalala mumtima mwake ndi vinyo,+ ine n’kukuuzani kuti, ‘Mukantheni Aminoni!’ pamenepo mumuphe. Musaope.+ Kodi si ndine amene ndakulamulani? Chitani zinthu mwamphamvu ndipo khalani olimba mtima.”
10 Pa tsiku la 7, pamene mtima wa mfumu unali kukondwera ndi vinyo,+ mfumu inauza Mehumani, Bizita, Haribona,+ Bigita, Abagata, Zetara ndi Karikasi, nduna 7 za panyumba ya mfumu zimene zinali kutumikira+ Mfumu Ahasiwero,
6 Anthu inu, perekani chakumwa choledzeretsa kwa munthu amene watsala pang’ono kuwonongedwa+ ndi vinyo kwa anthu amene mtima wawo ukuwawa.+
3 Ndinafufuza ndi mtima wanga wonse kuti ndidziwe uchitsiru posangalatsa thupi langa ndi vinyo,+ pamene ndinali kutsogolera mtima wanga ndi nzeru.+ Ndinachita zimenezi kuti ndione ubwino umene ana a anthu amapeza pa zimene amachita padziko lapansi pano masiku onse a moyo wawo.+
7 Pita ukadye chakudya chako mokondwera ndi kumwa vinyo wako ndi mtima wosangalala,+ chifukwa Mulungu woona wakondwera kale ndi ntchito zako.+
19 Chakudya chimachititsa antchito kuseka, ndipo vinyo amachititsa moyo kusangalala,+ koma ndalama zimathandiza pa zinthu zonse.+