Ekisodo 34:16 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 16 Kenako mudzatenga ena mwa ana awo aakazi kuti akhale akazi a ana anu aamuna,+ ndipo ana awo aakazi adzachita chiwerewere ndi milungu yawo, n’kuchititsa ana anu aamuna kuchita chiwerewere ndi milungu yawo.+ Levitiko 17:7 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 7 Chotero asamaperekenso nsembe zawo ku ziwanda zooneka ngati mbuzi*+ zimene akuchita nazo chiwerewere.+ Limeneli likhale lamulo kwa inu mpaka kalekale, m’mibadwo yanu yonse.”’ Numeri 15:39 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 39 ‘Chingwecho chikhale ngati mphonje kwa inu, kuti mukachiyang’ana muzikumbukira malamulo onse+ a Yehova ndi kuwasunga. Muleke kutsatira zilakolako za mitima yanu ndi maso anu,+ chifukwa potsatira zilakolako zimenezo, mukuchita chiwerewere.+ Yeremiya 3:9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 9 Iye anayamba kuchita uhule chifukwa choona nkhani imeneyi mopepuka. Anali kuipitsa dzikolo+ ndi kuchita chigololo ndi miyala komanso mitengo.+ Ezekieli 20:30 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 30 “Tsopano uza nyumba ya Isiraeli kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Kodi anthu inu mukudziipitsa potsatira njira za makolo anu?+ Kodi mukutsatira zinthu zawo zonyansa ndi kuchita zachiwerewere ndi mafano amenewo?+
16 Kenako mudzatenga ena mwa ana awo aakazi kuti akhale akazi a ana anu aamuna,+ ndipo ana awo aakazi adzachita chiwerewere ndi milungu yawo, n’kuchititsa ana anu aamuna kuchita chiwerewere ndi milungu yawo.+
7 Chotero asamaperekenso nsembe zawo ku ziwanda zooneka ngati mbuzi*+ zimene akuchita nazo chiwerewere.+ Limeneli likhale lamulo kwa inu mpaka kalekale, m’mibadwo yanu yonse.”’
39 ‘Chingwecho chikhale ngati mphonje kwa inu, kuti mukachiyang’ana muzikumbukira malamulo onse+ a Yehova ndi kuwasunga. Muleke kutsatira zilakolako za mitima yanu ndi maso anu,+ chifukwa potsatira zilakolako zimenezo, mukuchita chiwerewere.+
9 Iye anayamba kuchita uhule chifukwa choona nkhani imeneyi mopepuka. Anali kuipitsa dzikolo+ ndi kuchita chigololo ndi miyala komanso mitengo.+
30 “Tsopano uza nyumba ya Isiraeli kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Kodi anthu inu mukudziipitsa potsatira njira za makolo anu?+ Kodi mukutsatira zinthu zawo zonyansa ndi kuchita zachiwerewere ndi mafano amenewo?+