Genesis 1:26 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 26 Kenako Mulungu anati: “Tiyeni+ tipange munthu m’chifaniziro chathu,+ kuti akhale wofanana nafe.+ Ayang’anire nsomba zam’nyanja ndi zolengedwa zouluka m’mlengalenga, komanso nyama zoweta. Ayang’anirenso dziko lonse lapansi ndi nyama zonse zokwawa padziko lapansi.”+ Salimo 22:9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 9 Pakuti ndinu amene munanditulutsa m’mimba,+Amene munandichititsa kumva kuti ndine wotetezeka pamene ndinali kuyamwa mabere a mayi anga.+ Salimo 71:6 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 6 Kuyambira ndili m’mimba mwa mayi anga inu mwandithandiza.+Inu ndi amene munanditulutsa m’mimba mwa mayi anga.+Ndimatamanda inu nthawi zonse.+ Salimo 100:3 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 3 Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu.+Iye ndi amene anatipanga, sitinadzipange tokha.+Ndife anthu ake ndi nkhosa zimene akuweta.+ Yesaya 44:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Yehova, amene anakupanga+ ndiponso amene anakuumba,+ amene anali kukuthandiza ngakhale pamene unali m’mimba,+ wanena kuti, ‘Usachite mantha,+ iwe mtumiki wanga Yakobo, ndiponso iwe Yesuruni,+ amene ndakusankha. Yeremiya 1:5 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 5 “Ndisanakuumbe m’mimba,+ ndinakudziwa,+ ndipo usanatuluke m’mimbamo, ndinakusankha kuti uchite ntchito yopatulika.+ Ndinakusankha kuti ukhale mneneri ku mitundu ya anthu.”
26 Kenako Mulungu anati: “Tiyeni+ tipange munthu m’chifaniziro chathu,+ kuti akhale wofanana nafe.+ Ayang’anire nsomba zam’nyanja ndi zolengedwa zouluka m’mlengalenga, komanso nyama zoweta. Ayang’anirenso dziko lonse lapansi ndi nyama zonse zokwawa padziko lapansi.”+
9 Pakuti ndinu amene munanditulutsa m’mimba,+Amene munandichititsa kumva kuti ndine wotetezeka pamene ndinali kuyamwa mabere a mayi anga.+
6 Kuyambira ndili m’mimba mwa mayi anga inu mwandithandiza.+Inu ndi amene munanditulutsa m’mimba mwa mayi anga.+Ndimatamanda inu nthawi zonse.+
3 Dziwani kuti Yehova ndi Mulungu.+Iye ndi amene anatipanga, sitinadzipange tokha.+Ndife anthu ake ndi nkhosa zimene akuweta.+
2 Yehova, amene anakupanga+ ndiponso amene anakuumba,+ amene anali kukuthandiza ngakhale pamene unali m’mimba,+ wanena kuti, ‘Usachite mantha,+ iwe mtumiki wanga Yakobo, ndiponso iwe Yesuruni,+ amene ndakusankha.
5 “Ndisanakuumbe m’mimba,+ ndinakudziwa,+ ndipo usanatuluke m’mimbamo, ndinakusankha kuti uchite ntchito yopatulika.+ Ndinakusankha kuti ukhale mneneri ku mitundu ya anthu.”