Yobu 24:24 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 24 Oipawo amakhala okwezeka kwa kanthawi, kenako n’kutha.+Iwo amatsitsidwa,+ ndipo mofanana ndi wina aliyense amathotholedwa.Amadulidwa mofanana ndi nsonga ya ngala za tirigu. Mlaliki 6:12 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 12 Ndani angadziwe zabwino zimene munthu angachite pa moyo wake,+ masiku onse a moyo wake wachabechabe, umene umakhala ngati mthunzi?+ Pakuti ndani angamuuze munthu zimene zidzachitike padziko lapansi pano iyeyo atafa?+ Luka 12:20 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 20 Koma Mulungu anamuuza kuti, ‘Wopanda nzeru iwe, usiku womwe uno moyo wako adzaufuna.+ Nanga chuma chimene waunjikachi chidzakhala cha ndani?’+ Yakobo 1:11 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 11 Dzuwa limatuluka ndi kutentha kwake n’kufotetsa zomera, ndipo maluwa a zomerazo amathothoka. Kukongola kwake kumatha. Momwemonso munthu wachuma adzafa akutsatira njira ya moyo wake.+ 2 Petulo 2:3 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 3 Komanso chifukwa chosirira mwansanje, adzakudyerani masuku pamutu ndi mawu achinyengo.+ Koma chiweruzo chawo chimene chinagamulidwa kalekale+ chikubwera mofulumira, ndipo chiwonongeko chawo sichikuzengereza.+
24 Oipawo amakhala okwezeka kwa kanthawi, kenako n’kutha.+Iwo amatsitsidwa,+ ndipo mofanana ndi wina aliyense amathotholedwa.Amadulidwa mofanana ndi nsonga ya ngala za tirigu.
12 Ndani angadziwe zabwino zimene munthu angachite pa moyo wake,+ masiku onse a moyo wake wachabechabe, umene umakhala ngati mthunzi?+ Pakuti ndani angamuuze munthu zimene zidzachitike padziko lapansi pano iyeyo atafa?+
20 Koma Mulungu anamuuza kuti, ‘Wopanda nzeru iwe, usiku womwe uno moyo wako adzaufuna.+ Nanga chuma chimene waunjikachi chidzakhala cha ndani?’+
11 Dzuwa limatuluka ndi kutentha kwake n’kufotetsa zomera, ndipo maluwa a zomerazo amathothoka. Kukongola kwake kumatha. Momwemonso munthu wachuma adzafa akutsatira njira ya moyo wake.+
3 Komanso chifukwa chosirira mwansanje, adzakudyerani masuku pamutu ndi mawu achinyengo.+ Koma chiweruzo chawo chimene chinagamulidwa kalekale+ chikubwera mofulumira, ndipo chiwonongeko chawo sichikuzengereza.+