-
Yeremiya 31:12Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
12 Pamenepo iwo adzabwera ndi kufuula mosangalala pamwamba pa phiri la Ziyoni.+ Nkhope zawo zidzawala chifukwa cha ubwino wa Yehova.+ Zidzawalanso chifukwa cha mbewu, vinyo watsopano,+ mafuta, ana a nkhosa ndi ana a ng’ombe.+ Moyo wawo udzakhala ngati munda wothiriridwa bwino+ ndipo sadzakhalanso ofooka.”+
-
-
Yeremiya 33:11Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
11 M’malo amenewa mudzamveka mawu achikondwerero ndi achisangalalo.+ Mudzamveka mawu a mkwati ndi mawu a mkwatibwi, ndi mawu a anthu onena kuti: “Tamandani Yehova wa makamu, pakuti Yehova ndi wabwino.+ Kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale!”’+
“‘Anthuwo azidzabweretsa nsembe yoyamikira kunyumba ya Yehova,+ pakuti ndidzabwezeretsa anthu a m’dzikoli amene anagwidwa ndi kutengedwa kupita kudziko lina kuti akhalenso ngati mmene analili poyamba,’+ watero Yehova.”
-