Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yesaya 12:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 M’tsiku limenelo+ ndithu udzanena kuti: “Ndikukuthokozani inu Yehova pakuti ngakhale munandikwiyira, mkwiyo wanu unabwerera pang’onopang’ono+ ndipo munanditonthoza.+

  • Yesaya 40:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Iwe mkazi amene ukubweretsa uthenga wabwino wonena za Ziyoni,+ kwera phiri lalitali.+ Lankhula mwamphamvu ndiponso mofuula, iwe mkazi amene ukubweretsa uthenga wabwino wonena za Yerusalemu.+ Fuula! Usachite mantha.+ Uza mizinda ya ku Yuda kuti: “Uyu ndiye Mulungu wanu.”+

  • Yeremiya 31:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Pamenepo iwo adzabwera ndi kufuula mosangalala pamwamba pa phiri la Ziyoni.+ Nkhope zawo zidzawala chifukwa cha ubwino wa Yehova.+ Zidzawalanso chifukwa cha mbewu, vinyo watsopano,+ mafuta, ana a nkhosa ndi ana a ng’ombe.+ Moyo wawo udzakhala ngati munda wothiriridwa bwino+ ndipo sadzakhalanso ofooka.”+

  • Yeremiya 33:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 M’malo amenewa mudzamveka mawu achikondwerero ndi achisangalalo.+ Mudzamveka mawu a mkwati ndi mawu a mkwatibwi, ndi mawu a anthu onena kuti: “Tamandani Yehova wa makamu, pakuti Yehova ndi wabwino.+ Kukoma mtima kwake kosatha kudzakhalapobe mpaka kalekale!”’+

      “‘Anthuwo azidzabweretsa nsembe yoyamikira kunyumba ya Yehova,+ pakuti ndidzabwezeretsa anthu a m’dzikoli amene anagwidwa ndi kutengedwa kupita kudziko lina kuti akhalenso ngati mmene analili poyamba,’+ watero Yehova.”

  • Zekariya 2:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 “Fuula kwambiri ndi kusangalala, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni,+ pakuti ine ndikubwera+ ndipo ndidzakhala mwa iwe,”+ watero Yehova.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena