29 “Tamva za kunyada kwa Mowabu.+ Iye ndi wodzikuza kwambiri. Tamva za kudzikweza kwake, kunyada kwake, kudzikuza kwake ndi kudzitukumula kwa mtima wake.”+
37 “Tsopano ine Nebukadinezara ndikutamanda, kukweza ndi kulemekeza Mfumu yakumwamba,+ chifukwa ntchito zake zonse ndizo choonadi, njira zake ndi zolungama,+ ndiponso amatha kutsitsa anthu onyada.”+