-
Yesaya 14:2Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
2 Anthu a mitundu ina adzawatenga n’kubwerera nawo kwawo ndipo nyumba ya Isiraeli idzatenga anthuwo kuti akhale awo m’dziko la Yehova, ndiponso kuti akhale antchito awo aamuna ndi aakazi.+ Iwo adzagwira+ anthu amene anawagwira n’kupita nawo kudziko lina ndipo azidzalamulira anthu amene anali kuwagwiritsa ntchito.+
-
-
Yesaya 45:14Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
14 Yehova wanena kuti: “Antchito osalipidwa a ku Iguputo,+ amalonda a ku Itiyopiya, ndi Asabeya,+ amuna ataliatali,+ adzabwera kwa iwe ndipo adzakhala ako.+ Iwo adzayenda pambuyo pako. Adzabwera kwa iwe atamangidwa m’matangadza+ ndipo adzakugwadira.+ Adzapemphera kwa iwe kuti, ‘Zoonadi Mulungu ali ndi iwe+ ndipo palibenso wina. Palibenso Mulungu wina.’”+
-
-
Yeremiya 16:19Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
19 Inu Yehova, ndinu mphamvu yanga, malo anga achitetezo ndi malo anga othawirako pa tsiku la tsoka.+ Mitundu ya anthu idzabwera kwa inu kuchokera kumalekezero a dziko lapansi,+ ndipo idzati: “Ndithudi makolo athu analandira mafano* monga cholowa chawo.+ Analandira zinthu zachabechabe ndi zinthu zosapindulitsa.”+
-