14 Yehova, Wokuwombolani,+ Woyera wa Isiraeli,+ wanena kuti: “Chifukwa cha inu, ndidzawatumiza ku Babulo. Ndidzachititsa kuti zitsulo za ndende zimasuke+ ndiponso ndidzagonjetsa Akasidi amene ali m’zombo ndi kuwachititsa kulira mokuwa.+
25 “Yehova watsegula nkhokwe yake ya zida ndipo akutulutsamo zida zake zodzudzulira mwamphamvu.+ Akutero chifukwa chakuti Yehova wa makamu, Ambuye Wamkulu Koposa,+ ali ndi ntchito yoti achite m’dziko la Akasidi.+