11 Ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova. Ndatopa ndi kukhala chete.”+
“Tsanulira mkwiyowo pa mwana amene ali mumsewu+ ndipo nthawi yomweyo uutsanulirenso pa kagulu ka anyamata okondana. Mwamuna pamodzi ndi mkazi wake, munthu wachikulire pamodzi ndi munthu wokalamba, onsewo adzagwidwa.+