-
Yesaya 63:1Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
63 Kodi amene akuchokera ku Edomuyu+ ndi ndani, amene akuchokera ku Bozira+ atavala zovala zowala zamitundumitundu, amene zovala zake ndi zolemekezeka, ndiponso amene akuyenda mwamphamvu chifukwa cha kuchuluka kwa mphamvu zake?
“Ndi ine, amene ndimalankhula mwachilungamo,+ amene ndili ndi mphamvu zambiri zopulumutsa.”+
-
-
Yeremiya 49:2Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
2 “‘Choncho taonani! Masiku adzafika,’ watero Yehova, ‘ndipo Raba,+ umene ndi mzinda wa ana a Amoni, ndidzaulizira chizindikiro chakuti kukubwera nkhondo.+ Ndipo mzindawu udzasanduka bwinja ndi mulu wadothi.+ Midzi yake yozungulira+ idzatenthedwa.’+
“‘Isiraeli adzatenga dziko la anthu amene analanda dziko lake,’+ watero Yehova.
-