4 Pakuti inu mwakhala malo achitetezo kwa munthu wonyozeka ndiponso malo achitetezo kwa munthu wosauka m’masautso ake.+ Mwakhala malo ousapo mvula yamkuntho ndi mthunzi+ wobisalirapo kutentha kwa dzuwa. Mwakhala wotero pamene anthu ankhanza akuwomba anzawo ngati mvula yamkuntho yowomba khoma.
22 Ine ndidzamuweruza+ ndi mliri+ ndiponso magazi.+ Ndidzamugwetsera mvula yamphamvu, matalala,+ moto+ ndi sulufule. Ndidzagwetsa zimenezi pa iyeyo, pagulu lake la asilikali ndi pa mitundu yambiri ya anthu amene adzakhale kumbali yake.+