9 kuti ndiuze akaidi+ kuti, ‘Tulukani!’+ ndi amene ali mu mdima+ kuti, ‘Dziululeni!’+ Iwo adzadya msipu m’mphepete mwa msewu, ndipo m’mphepete mwa njira zonse zodutsidwadutsidwa mudzakhala malo awo odyeramo msipu.+
14 Weta anthu ako ndi ndodo yako.+ Weta gulu la nkhosa zomwe ndi cholowa chako, zimene zinali kukhala zokhazokha m’nkhalango pakati pa mitengo ya zipatso.+ Uzilole kuti zikadyere ku Basana ndi ku Giliyadi+ ngati mmene zinali kuchitira masiku akale.+