7 Nkhosa zonse za ku Kedara+ zidzasonkhanitsidwa kwa iwe. Nkhosa zamphongo za ku Nebayoti+ zidzakutumikira.+ Ine ndidzazilandira paguwa langa lansembe,+ ndipo ndidzakongoletsa nyumba yanga yokongola.+
11 “Mitundu yambiri ya anthu idzadziphatika kwa Yehova pa tsikulo,+ choncho adzakhala anthu anga.+ Ine ndidzakhala mwa iwe.” Ndipo udzadziwa kuti Yehova wa makamu wandituma kwa iwe.+