24 Kenako mfumu ya Asuri inatenga anthu kuchokera ku Babulo,+ Kuta, Ava,+ Hamati,+ ndi Sefaravaimu+ n’kuwakhazika m’mizinda ya Samariya,+ m’malo mwa ana a Isiraeli. Anthuwo anatenga Samariya n’kumakhala m’mizinda yake.
3 Koma Zerubabele, Yesuwa,+ ndi atsogoleri ena onse+ a nyumba za makolo za Isiraeli anawayankha kuti: “Mulibe ufulu womanga nafe limodzi nyumba ya Mulungu wathu,+ pakuti ifeyo patokha timangira limodzi nyumba ya Yehova Mulungu wa Isiraeli, monga momwe Mfumu Koresi+ ya Perisiya yatilamulira.”