Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 14:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Pambuyo pake, atauza anthuwo kuti azipita, anakwera m’phiri yekhayekha kukapemphera.+ Ngakhale kuti kunali kutada, iye anakhalabe kumeneko yekhayekha.

  • Maliko 6:45
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 45 Kenako mwamsanga, Yesu analimbikitsa ophunzira ake kuti akwere ngalawa ndi kutsogola kupita kutsidya lina loyang’anizana nalo cha ku Betsaida. Koma iye anatsalira akuuza anthuwo kuti azipita kwawo.+

  • Yohane 17:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Iwo sali mbali ya dziko,+ monganso ine sindili mbali ya dziko.+

  • Yohane 18:36
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 36 Yesu anayankha kuti:+ “Ufumu wanga suli mbali ya dziko lino.+ Ufumu wanga ukanakhala mbali ya dziko lino, atumiki anga akanamenya nkhondo+ kuti ndisaperekedwe kwa Ayuda. Koma ufumu wanga si wochokera pansi pano ayi.”

  • Yakobo 1:27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Kupembedza koyera+ ndi kosaipitsidwa+ kwa Mulungu ndi Atate wathu ndi uku: Kusamalira ana amasiye+ ndi akazi amasiye+ m’masautso awo,+ ndi kukhala wopanda banga+ la dzikoli.+

  • Yakobo 4:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Achigololo+ inu, kodi simukudziwa kuti kuchita ubwenzi ndi dziko n’kudziika pa udani ndi Mulungu?+ Choncho, aliyense amene akufuna kukhala bwenzi+ la dziko akudzisandutsa mdani wa Mulungu.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena