Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 29:10-14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Kenako ubweretse ngʼombe patsogolo pa chihema chokumanako, ndipo Aroni ndi ana ake aike manja awo pamutu wa ngʼombeyo.+ 11 Ndiyeno ngʼombeyo uiphe pamaso pa Yehova, pakhomo la chihema chokumanako.+ 12 Ukatero utengeko magazi a ngʼombeyo ndi chala chako ndipo uwapake panyanga za guwa lansembe.+ Magazi otsalawo uwathire pansi pa guwa lansembe.+ 13 Kenako utenge mafuta onse+ okuta matumbo, mafuta apachiwindi, impso ziwiri ndi mafuta ake nʼkuzitentha kuti paguwa lansembe pakhale utsi.+ 14 Koma nyama ya ngʼombeyo, chikopa chake ndi ndowe zake uzitenthe ndi moto kunja kwa msasa. Ngʼombeyo ndi nsembe yamachimo.

  • Levitiko 4:3, 4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Ngati wansembe wodzozedwa+ wachita tchimo+ ndipo lapangitsa anthu onse kupalamula, azipereka kwa Yehova ngʼombe yaingʼono yamphongo yopanda chilema monga nsembe yamachimo chifukwa cha tchimo lakelo.+ 4 Azibweretsa ngʼombe yamphongoyo pamaso pa Yehova pakhomo la chihema chokumanako+ ndipo aziika dzanja lake pamutu wa ngʼombeyo, kenako aziipha pamaso pa Yehova.+

  • Levitiko 16:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Akatero Aroni azibweretsa ngʼombe yamphongo ya nsembe yake yamachimo, ndipo aziphimba machimo ake+ ndi a banja lake.*

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena