Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yobu 21:19, 20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Mulungu adzalanga ana a munthu woipa chifukwa cha zolakwa za bambo awo.

      Koma Mulungu amulangenso iyeyo kuti adziwe kulakwa kwake.+

      20 Maso ake aone iye akamawonongedwa,

      Ndipo adzamwe mkwiyo wa Wamphamvuyonse.+

  • Yeremiya 25:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Yehova Mulungu wa Isiraeli anandiuza kuti: “Tenga kapu iyi ya vinyo wa mkwiyo imene ili mʼdzanja langa ndipo ukamwetse mitundu yonse imene ndikukutumizako.

  • Yeremiya 25:28
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 28 Ngati angakakane kulandira kapuyi mʼmanja mwako kuti amwe, ukawauze kuti, ‘Yehova wa magulu ankhondo akumwamba wanena kuti: “Mukuyenera kumwa basi.

  • Yeremiya 49:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Yehova wanena kuti: “Taonani! Ngati amene sanapatsidwe chiweruzo kuti amwe zamʼkapu akuyenera kumwa, kodi iweyo ukuyenera kusiyidwa osapatsidwa chilango? Ayi, sudzasiyidwa osapatsidwa chilango chifukwa ukuyenera kumwa zamʼkapumo.”+

  • Chivumbulutso 14:9, 10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Mngelo wina wachitatu anawatsatira ndipo ankanena mofuula kuti: “Ngati wina walambira chilombo+ ndi chifaniziro chake ndipo walandira chizindikiro pachipumi kapena padzanja lake,+ 10 adzamwanso vinyo wosasungunula wa mkwiyo wa Mulungu amene akuthiridwa mʼkapu ya mkwiyo wake.+ Ndipo adzazunzidwa ndi moto ndi sulufule+ pamaso pa angelo oyera komanso pamaso pa Mwanawankhosa.

  • Chivumbulutso 16:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Mzinda waukulu+ unagawika zigawo zitatu ndipo mizinda ya mitundu ya anthu inagwa. Ndiyeno Mulungu anakumbukira Babulo Wamkulu,+ kuti amupatse kapu imene inali ndi vinyo wa mkwiyo wake waukulu.+

  • Chivumbulutso 18:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Mubwezereni zofanana ndi zimene iye anachitira ena.+ Mubwezereni kuwirikiza kawiri zinthu zimene iyeyo anachita.+ Mʼkapu+ imene anaikamo chakumwa chosakaniza, ikanimo chakumwa chakecho kuwirikiza kawiri.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena