-
Maliko 3:1-6Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
3 Kachiwirinso Yesu analowa musunagoge. Mmenemo munali munthu wolumala dzanja.+ 2 Ndiyeno Afarisi ankamuyangʼanitsitsa kuti aone ngati angachiritse munthuyo pa Sabata nʼcholinga choti amuimbe mlandu. 3 Ndipo iye anauza munthu wolumala dzanjayo kuti: “Nyamuka, bwera pakatipa.” 4 Kenako anawafunsa kuti: “Kodi malamulo amalola kuchita chiyani pa Sabata, chabwino kapena choipa? Kupulumutsa moyo kapena kupha?”+ Koma iwo anangokhala chete. 5 Yesu anawayangʼana mokwiya ndipo anamva chisoni kwambiri chifukwa cha kuuma mtima kwawo.+ Kenako anauza munthuyo kuti: “Tambasula dzanja lako.” Iye analitambasuladi ndipo linakhala labwinobwino. 6 Ataona zimenezi Afarisiwo anatuluka ndipo nthawi yomweyo anapita kukakonza chiwembu limodzi ndi anthu amene ankatsatira Herode+ kuti amuphe.
-
-
Luka 6:6-11Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
6 Tsiku linanso la sabata,+ iye analowa musunagoge nʼkuyamba kuphunzitsa. Mmenemo munali munthu amene dzanja lake lamanja linali lolumala.+ 7 Alembi ndi Afarisi ankamuyangʼanitsitsa kuti aone ngati angachiritse munthuyo pa Sabata nʼcholinga choti amuimbe mlandu. 8 Koma iye anadziwa zimene iwo ankaganiza.+ Choncho anauza munthu wolumala dzanjayo kuti: “Nyamuka, bwera pakatipa.” Munthuyo ananyamuka nʼkuima pamenepo. 9 Kenako Yesu anawafunsa kuti: “Kodi malamulo amalola kuchita chiyani pa Sabata, chabwino kapena choipa? Kupulumutsa moyo kapena kupha?”+ 10 Atayangʼana uku ndi uku, anauza munthu uja kuti: “Tambasula dzanja lako.” Iye analitambasuladi ndipo linakhalanso labwinobwino. 11 Koma iwo anakwiya kwambiri ndipo anayamba kukambirana zoti amuchite Yesu.
-