Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 3/98 tsamba 6
  • Zokumbutsa za Chikumbutso

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zokumbutsa za Chikumbutso
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—1998
  • Nkhani Yofanana
  • Zofunika Kukumbukira Panthaŵi ya Chikumbutso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
  • Zokumbutsa za Chikumbutso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
  • Zikumbutso za pa Chikumbutso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1997
  • Zofunika Kukumbukira pa Chikumbutso
    Utumiki wathu wa Ufumu—2002
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—1998
km 3/98 tsamba 6

Zokumbutsa za Chikumbutso

Chikumbutso chidzakhalako Loŵeruka, pa April 11. Akulu asamalire zotsatirazi:

◼ Poika nthaŵi ya msonkhanowo, onani kuti zizindikiro zisadzayambe kuperekedwa mpaka dzuŵa litaloŵa.

◼ Aliyense, kuphatikizapo wokamba nkhani, ayenera kuuzidwa nthaŵi yeniyeni ndi malo ake.

◼ Mudzapezeretu mkate ndi vinyo woyenera nkukhala nazo chire.—Onani Nsanja ya Olonda ya February 15, 1985 (Chingelezi), tsamba 19.

◼ Mbale, magalasi, ndi thebulo yabwino ndi nsalu yapathebulo mudzabwere nazo ku holo nkuziyala pasadakhale.

◼ Nyumba ya Ufumu kapena malo ena osonkhanira ayenera kudzayeretsedwa pasadakhale.

◼ Akalinde ndi otumikira ayenera kusankhidwa ndi kulangizidwa pasadakhale za mmene adzayendetsera zinthu ndi ntchito zawo.

◼ Mupange makonzedwe okaperekera zizindikirozo kwa wodzozedwa aliyense wofooka amene sangathe kupezekapo.

◼ Ngati mipingo ingapo idzagwiritsira ntchito Nyumba ya Ufumu imodzimodziyo, mipingoyo idzagwirizane bwino za nthaŵi, kotero kuti pasadzakhale kupanikizana kwa anthu pakhonde, pakhomo, koimika magalimoto.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena