Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 3/15 tsamba 1
  • Kodi Mwayamba Kukonzekera Chikumbutso?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mwayamba Kukonzekera Chikumbutso?
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Mukukonzekera Chikumbutso?
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2021
  • Khalani ndi Mtima Wosangalala Pokonzekera Chikumbutso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Zofunika Kukumbukira Panthaŵi ya Chikumbutso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
  • Zokumbutsa za Chikumbutso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1998
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
km 3/15 tsamba 1

Kodi Mwayamba Kukonzekera Chikumbutso?

Pa Nisani 13, mu 33 C.E., Yesu ankadziwa kuti wangotsala ndi usiku umodzi wokha woti akhale ndi atumwi ake. Ankafunika kuchita Pasika womaliza, kenako n’kuyambitsa mwambo wofunika kwambiri, wa Chakudya Chamadzulo cha Ambuye. Kuti zonsezi zitheke, ankafunika kukonzekera. Choncho anatumiza Petulo ndi Yohane kuti akakonze zonse zofunika pa mwambowu. (Luka 22:7-13) Kuyambira nthawi imeneyo, chaka chilichonse Akhristu amachita mwambo umenewu, koma amafunika kukonzekera. (Luka 22:19) Kodi tingakonzekere bwanji mwambo wa Chikumbutso wachaka chino, womwe udzachitike pa 3 April?

Zimene Akulu Angachite

  • Kambiranani ngati Chikumbutso chidzachitikire m’Nyumba ya Ufumu kapena pamalo ena. Onetsetsani kuti padzakhala malo okwanira, powala bwino komanso podutsa mphepo yokwanira. Konzani zoti malowa adzayeretsedwe bwino nthawi idakalipo.

  • Sankhani wokamba nkhani ya Chikumbutso woyenerera, tcheyamani komanso abale oti adzapemphere pa nthawi yoyendetsa zizindikiro.

  • Ngati mipingo ingapo idzachite Chikumbutso pamalo amodzi pa nthawi zosiyana, kambiranani za nthawi yoyambira, koimika magalimoto komanso zokhudza mmene anthu adzalowere ndi kutuluka.

  • Sankhani abale omwe adzakhale olandira alendo komanso oyendetsa zizindikiro n’kuwauza zoyenera kuchita.

  • Kambiranani mmene mungapezere zizindikiro, mbale, matambula, tebulo loyenera komanso nsalu yoyala patebulopo.

Zimene Ofalitsa Angachite

  • Konzani zoti mudzagwire nawo mwakhama ntchito yoitanira anthu ku Chikumbutso.

  • Lembani mayina a ophunzira Baibulo, achibale, anzanu akusukulu, akuntchito komanso anthu ena omwe mukufuna kudzawaitanira ku Chikumbutso.

  • Werengani malemba a pa nthawi ya Chikumbutso ndi kuwaganizira mozama.

  • Mudzafike mofulumira kuti mudzalandire alendo obwera ku mwambowu.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena