Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 9/15 tsamba 4
  • Zitsanzo za Ulaliki

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zitsanzo za Ulaliki
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Nkhani Yofanana
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Zitsanzo za Ulaliki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2012
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
km 9/15 tsamba 4

Zitsanzo za Ulaliki

Nsanja ya Olonda October 1

“Tikugawira anthu m’dera lino magazini iyi. [Asonyezeni Nsanja ya Olonda ya October 1.] Anthu ena amaganiza kuti kupemphera n’kungotaya nthawi chifukwa palibe aliyense amene amamvetsera mapempherowo. Koma anthu ena amakhulupirira kuti Mulungu amamvetsera mapemphero awo. Kodi inuyo mukuganiza bwanji? [Yembekezerani ayankhe.] Taonani zimene Baibulo limanena pa nkhaniyi. [Werengani Yesaya 30:19.] M’magazini iyi muli mfundo zomwe zikusonyeza kuti Mulungu amamva ndiponso kuyankha mapemphero ngati munthu wapemphera moyenera komanso wapempha zinthu zoyenera.”

Galamukani! October

“Anthu ambiri amadabwa kuti n’chifukwa chiyani Mulungu amalola kuti anthu azivutika. Kodi mukuganiza kuti n’kupanda ulemu kufunsa Mulungu funso limeneli? [Yembekezerani ayankhe.] Nayenso Yobu, yemwe anali munthu wolungama, ankaona kuti atapeza mwayi wofunsa Mulungu, akanamufunsa mafunso omwe ankafuna kudziwa mayankho ake. [Werengani Yobu 23:3-5.] Magaziniyi ili ndi mayankho a m’Baibulo a mafunso atatu amene anthu ambiri, atapatsidwa mwayi, angakonde kumufunsa Mulungu.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena