7 Atatero anaveka Aroni mkanjo+ ndi kum’manga lamba wa pamimba.+ Anamuvekanso malaya odula manja+ komanso efodi,*+ ndi kum’manga kwambiri ndi lamba+ wa efodiyo.
13 Kenako Mose anaitana ana a Aroni+ ndi kuwaveka mikanjo, kuwamanga malamba a pamimba,+ ndi kuwakulunga mipango+ kumutu, monga mmene Yehova analamulira Mose.