Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 8:22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 Pa tsiku limenelo ndidzapatula dera la Goseni kumene kuli anthu anga, kuti kusakhale tizilombo toyamwa magazi.+ Ndidzatero kuti udziwe kuti ine ndine Yehova, ndipo ndili ndi mphamvu padziko lonse lapansi.+

  • Ekisodo 10:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Anthu sanathe kuonana ndipo palibe anachoka pakhomo pake kwa masiku atatu. Koma kumene ana onse a Isiraeli anali kukhala kunali kuwala.+

  • Ekisodo 11:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Koma galu sadzauwa aliyense wa ana a Isiraeli, sadzauwa munthu kapena chiweto,+ kuti mudziwe kuti Yehova akhoza kuchitira ana a Isiraeli zinthu zosiyana ndi zimene angachitire Aiguputo.’+

  • Ekisodo 12:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Magaziwo adzakhala chizindikiro panyumba zimene mudzakhalamo. Ndipo ine ndidzaona magaziwo ndi kukupitirirani,+ choncho mliri sudzakugwerani ndi kukuwonongani pamene ndikukantha dziko la Iguputo.

  • Yesaya 65:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Chotero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Atumiki anga adzadya,+ koma inuyo mudzakhala ndi njala.+ Atumiki anga adzamwa,+ koma inuyo mudzakhala ndi ludzu.+ Atumiki anga adzasangalala,+ koma inuyo mudzachita manyazi.+

  • Malaki 3:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Ndithu, anthu inu mudzaonanso kusiyana pakati pa munthu wolungama ndi woipa+ ndiponso pakati pa munthu amene akutumikira Mulungu ndi amene sanatumikirepo Mulungu.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena