2 Nayi mbiri ya Yakobo.
Pamene Yosefe+ anali ndi zaka 17, tsiku lina anapita kokadyetsa nkhosa limodzi ndi abale ake.+ Pokhala wamng’ono, anali limodzi ndi ana a Biliha+ ndi ana a Zilipa,+ omwe anali akazi a bambo ake. Tsopano Yosefe anakauza bambo ake zoipa zimene abale ake anali kuchita.+