Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Genesis 37:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Nayi mbiri ya Yakobo.

      Pamene Yosefe+ anali ndi zaka 17, tsiku lina anapita kokadyetsa nkhosa limodzi ndi abale ake.+ Pokhala wamng’ono, anali limodzi ndi ana a Biliha+ ndi ana a Zilipa,+ omwe anali akazi a bambo ake. Tsopano Yosefe anakauza bambo ake zoipa zimene abale ake anali kuchita.+

  • 1 Samueli 2:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Musatero+ ana anga, chifukwa nkhani imene ndikumva, imene anthu a Yehova akufalitsa, si yabwino ayi.+

  • Esitere 6:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 M’bukumo anapeza kuti mwalembedwa zimene Moredekai anaulula+ zokhudza Bigitana ndi Teresi, nduna ziwiri+ za panyumba ya mfumu, alonda apakhomo, amene anafuna kupha Mfumu Ahasiwero.

  • Miyambo 29:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Wochita ubwenzi ndi mbala akudana ndi moyo wake.+ Iye angamve lumbiro lokhudza temberero, koma osakanena chilichonse.+

  • 1 Akorinto 1:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Pakuti a m’banja la Kuloe andiuza+ za inu, abale anga, kuti pali magawano pakati panu.

  • 1 Akorinto 5:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Mbiri yamvekatu kuti pakuchitika dama*+ pakati panu, ndipo dama lake ndi loti ngakhale anthu a mitundu ina sachita. Akuti mwamuna wina watengana ndi mkazi wa bambo ake.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena