Numeri 22:6 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 6 Tsopano tabwerani chonde, mudzanditembererere+ anthuwa chifukwa ndi amphamvu kuposa ineyo, kuti mwina ndingawagonjetse n’kuwapitikitsa m’dziko lino. Ndikudziwa kuti munthu amene inu mwamudalitsa, amakhaladi wodalitsika, ndipo munthu amene mwamutemberera, amakhaladi wotembereredwa.”+ Numeri 23:7 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 7 Pamenepo Balamu anayamba kulankhula mwa ndakatulo,+ kuti:“Balaki mfumu ya Mowabu yandiitana kuchokera ku Aramu,+Kuchokera kumapiri a kum’mawa, kuti:‘Bwera, udzanditembererere Yakobo.Bwera, udzaitanire tsoka pa Isiraeli.’+ Numeri 23:11 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 11 Balaki atamva zimenezi anafunsa Balamu kuti: “N’chiyani mwandichitachi? Ndinakutengani kuti mudzatemberere adani anga, koma inu mwawadalitsa kwambiri.”+ Numeri 24:10 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 10 Pamenepo Balaki anapsera mtima Balamu n’kuwomba m’manja.+ Kenako anauza Balamu kuti: “Ndinakuitana kuti udzatemberere+ adani anga, koma iwe wawadalitsa kwambiri katatu konseka!
6 Tsopano tabwerani chonde, mudzanditembererere+ anthuwa chifukwa ndi amphamvu kuposa ineyo, kuti mwina ndingawagonjetse n’kuwapitikitsa m’dziko lino. Ndikudziwa kuti munthu amene inu mwamudalitsa, amakhaladi wodalitsika, ndipo munthu amene mwamutemberera, amakhaladi wotembereredwa.”+
7 Pamenepo Balamu anayamba kulankhula mwa ndakatulo,+ kuti:“Balaki mfumu ya Mowabu yandiitana kuchokera ku Aramu,+Kuchokera kumapiri a kum’mawa, kuti:‘Bwera, udzanditembererere Yakobo.Bwera, udzaitanire tsoka pa Isiraeli.’+
11 Balaki atamva zimenezi anafunsa Balamu kuti: “N’chiyani mwandichitachi? Ndinakutengani kuti mudzatemberere adani anga, koma inu mwawadalitsa kwambiri.”+
10 Pamenepo Balaki anapsera mtima Balamu n’kuwomba m’manja.+ Kenako anauza Balamu kuti: “Ndinakuitana kuti udzatemberere+ adani anga, koma iwe wawadalitsa kwambiri katatu konseka!