Deuteronomo 21:9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 9 Ndipo inuyo mudzachotsa mlandu wa magazi a munthu wosalakwa pakati panu,+ chifukwa mudzakhala mutachita choyenera pamaso pa Yehova.+ 2 Mafumu 21:16 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 16 Manase anakhetsanso magazi osalakwa ochuluka zedi,+ mpaka magaziwo anadzaza nawo Yerusalemu kuyambira koyambirira mpaka kumapeto, kuwonjezera pa tchimo lake limene anachimwitsa nalo Yuda mwa kuchita zoipa pamaso pa Yehova.+ Miyambo 6:17 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 17 Maso odzikweza,+ lilime lonama,+ manja okhetsa magazi a anthu osalakwa,+ Yeremiya 7:6 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 6 ngati simudzapondereza mlendo wokhala pakati panu, mwana wamasiye* ndi mkazi wamasiye,+ komanso ngati simudzakhetsa magazi a munthu wopanda mlandu m’dziko lino,+ ndiponso ngati simudzatsatira milungu ina, zimene zingakubweretsereni tsoka,+ Yona 1:14 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 14 Pamenepo anthuwo anafuulira Yehova ndi kunena kuti:+ “Chonde inu Yehova, musalole kuti tiwonongeke chifukwa cha munthu uyu! Musaike pa ife mlandu wa magazi a munthu wosalakwa,+ chifukwa zonsezi zachitika pokwaniritsa chifuniro chanu, inu Yehova!”+ Mateyu 27:4 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 4 Iye anati: “Ndachimwa popereka munthu wolungama.”*+ Koma iwo anamuyankha kuti: “Ife sizikutikhudza zimenezo. Udziwa wekha chochita!”+
9 Ndipo inuyo mudzachotsa mlandu wa magazi a munthu wosalakwa pakati panu,+ chifukwa mudzakhala mutachita choyenera pamaso pa Yehova.+
16 Manase anakhetsanso magazi osalakwa ochuluka zedi,+ mpaka magaziwo anadzaza nawo Yerusalemu kuyambira koyambirira mpaka kumapeto, kuwonjezera pa tchimo lake limene anachimwitsa nalo Yuda mwa kuchita zoipa pamaso pa Yehova.+
6 ngati simudzapondereza mlendo wokhala pakati panu, mwana wamasiye* ndi mkazi wamasiye,+ komanso ngati simudzakhetsa magazi a munthu wopanda mlandu m’dziko lino,+ ndiponso ngati simudzatsatira milungu ina, zimene zingakubweretsereni tsoka,+
14 Pamenepo anthuwo anafuulira Yehova ndi kunena kuti:+ “Chonde inu Yehova, musalole kuti tiwonongeke chifukwa cha munthu uyu! Musaike pa ife mlandu wa magazi a munthu wosalakwa,+ chifukwa zonsezi zachitika pokwaniritsa chifuniro chanu, inu Yehova!”+
4 Iye anati: “Ndachimwa popereka munthu wolungama.”*+ Koma iwo anamuyankha kuti: “Ife sizikutikhudza zimenezo. Udziwa wekha chochita!”+