16 Malirewo anatsetserekera kuphiri loyang’anizana ndi chigwa cha mwana wa Hinomu,+ limene linathera kumpoto kwa chigwa cha Arefai.+ Kenako anatsetserekera kuchigwa cha Hinomu kum’mwera kwa malo otsetsereka otchedwa Yebusi,+ n’kutsetserekabe mpaka ku Eni-rogeli.+
10 Mfumuyo inachititsa kuti ku Tofeti,+ m’chigwa cha ana a Hinomu+ kukhale kosayenera kulambirako, kuti munthu aliyense asawotcheko* mwana wake wamwamuna kapena mwana wake wamkazi pamoto,+ pomupereka kwa Moleki.+
31 Iwo amanga malo okwezeka ku Tofeti,+ m’chigwa cha mwana wa Hinomu,+ kuti azitentha ana awo aamuna ndi ana awo aakazi pamoto,+ chinthu chimene sindinawalamule kuchita ndiponso chimene sindinachiganizirepo mumtima mwanga.’+
22 Koma ine ndikukuuzani kuti aliyense wopitiriza kupsera mtima+ m’bale wake wapalamula mlandu+ wa kukhoti. Komano aliyense wonenera m’bale wake mawu achipongwe wapalamula mlandu wa ku Khoti Lalikulu. Ndipo aliyense wonena mnzake kuti, ‘Chitsiru iwe!’ adzapita ku Gehena* wamoto.+