Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Genesis 14:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Chotero Abulamu anamva kuti m’bale wake wagwidwa+ ndipo akupita naye kudziko lina. Atamva zimenezo iye anasonkhanitsa anyamata ake odziwa kumenya nkhondo.+ Anali akapolo ake okwanira 318, obadwira m’nyumba yake.+ Iwo analondola oukirawo mpaka ku Dani.+

  • Deuteronomo 34:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 Ndiyeno Mose anachoka m’chipululu cha Mowabu kupita m’phiri la Nebo,+ pamwamba pa Pisiga,+ moyang’anana ndi Yeriko.+ Pamenepo Yehova anayamba kumuonetsa dziko lonse, kuchokera ku Giliyadi mpaka ku Dani.+

  • Yoswa 19:47
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 47 Gawo la ana a Dani linawachepera,+ choncho anapita kukachita nkhondo ku Lesemu.+ Analanda mzindawo n’kupha anthu ake ndi lupanga. Kenako anautenga n’kuyamba kukhalamo ndipo anautcha Lesemu Dani, potengera dzina la kholo lawo Dani.+

  • Oweruza 20:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Chotero ana onse a Isiraeli anatuluka,+ kuchokera ku Dani+ mpaka kumunsi ku Beere-seba,+ ndipo khamu lonselo linasonkhana pamodzi mogwirizana+ kwa Yehova ku Mizipa,+ pamodzinso ndi anthu a m’dera la Giliyadi.+

  • 2 Samueli 17:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Ndiye ine malangizo anga ndi onena kuti: Sonkhanitsa ndithu Isiraeli yense pamaso pako kuyambira ku Dani mpaka ku Beere-seba.+ Akhale ochuluka ngati mchenga wa m’mphepete mwa nyanja,+ ndipo iweyo uwatsogolere kunkhondo.+

  • 1 Mafumu 12:29
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 29 Ndiyeno chifaniziro cha ng’ombe chimodzi anakachiika ku Beteli,+ china anakachiika ku Dani.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena