4 Ana a Yosefe anakhala mafuko awiri,+ la Manase+ ndi la Efuraimu.+ Iwowa anapatsa Alevi mizinda+ yoti azikhalamo, malo odyetserako ziweto, ndi osungirako katundu wawo, koma sanawagawire cholowa cha malo.+
16Malire a gawo+ la ana a Yosefe+ anayambira kumtsinje wa Yorodano+ kufupi ndi Yeriko kukafika kumadzi a Yeriko chakum’mawa, mpaka kuchipululu chochokera ku Yeriko kukafika kudera lamapiri la Beteli.+