Yoswa
16 Malire a gawo+ la ana a Yosefe+ anayambira kumtsinje wa Yorodano+ kufupi ndi Yeriko kukafika kumadzi a Yeriko chakum’mawa, mpaka kuchipululu chochokera ku Yeriko kukafika kudera lamapiri la Beteli.+ 2 Atachoka ku Beteli wa ku Luzi,+ malirewo anakadutsa kumalire a Aareki+ ku Ataroti. 3 Kenako anatsetserekera kumadzulo kumalire a Ayafeleti, mpaka kukafika kumalire a Beti-horoni Wakumunsi+ ndi Gezeri,+ n’kukathera kunyanja.+
4 Ana a Yosefe,+ omwe ndi Manase ndi Efuraimu,+ analandira gawo lawo.+ 5 Malire a kum’mawa a cholowa cha ana a Efuraimu potsata mabanja awo, anali Ataroti-adara+ mpaka kukafika ku Beti-horoni Wakumtunda,+ 6 n’kukathera kunyanja. Kumpoto kwake kunali Mikametatu,+ ndipo malirewo anazungulira chakum’mawa kukafika ku Taanatu-silo, n’kupitirirabe chakum’mawa mpaka ku Yanoa. 7 Ndiyeno anatsetsereka kuchoka ku Yanoa kukafika ku Ataroti ndi ku Naara mpaka ku Yeriko,+ n’kupitirirabe mpaka ku Yorodano. 8 Kuchoka ku Tapuwa,+ malirewo analowera chakumadzulo kuchigwa cha Kana+ n’kukathera kunyanja.+ Chimenechi ndi cholowa cha fuko la ana a Efuraimu potsata mabanja awo. 9 Cholowacho chinaphatikizapo mizinda yonse ndi midzi ya ana a Efuraimu+ imene inali mkati mwa cholowa cha ana a Manase.
10 Aefuraimu analephera kupitikitsa Akanani+ amene anali kukhala ku Gezeri.+ Choncho Akananiwo akukhalabe pakati pa Aefuraimu mpaka lero,+ ndipo anayamba kuwagwiritsa ntchito yaukapolo.+