2 Samueli 7:16 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 16 Nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhazikika pamaso pako mpaka kalekale. Mpando wako wachifumu udzakhazikika mpaka kalekale.”’”+ Salimo 72:17 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 17 Dzina lake likhalebe mpaka kalekale.+Nthawi zonse pamene dzuwa latuluka, dzina lake lizitchuka,Ndipo kudzera mwa iye, anthu apeze madalitso.*+Mitundu yonse ya anthu imutche wodala.+ Yesaya 11:1 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 11 Nthambi+ idzatuluka pachitsa cha Jese,+ ndipo mphukira+ yotuluka pamizu yake idzakhala yobereka zipatso.+ Yeremiya 23:5 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 5 “Taonani! Masiku adzafika,” watero Yehova, “ndipo Davide ndidzamuutsira mphukira yolungama.+ Ndithudi mfumu idzalamulira+ m’dzikoli ndi kuchita zinthu mozindikira, motsatira malamulo komanso mwachilungamo.+ Zekariya 6:13 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 13 Munthu ameneyu adzamanga kachisi wa Yehova ndipo adzalandira ulemerero.+ Iye azidzalamulira atakhala pampando wake wachifumu ndipo adzakhalanso wansembe ali pampando womwewo.+ Maudindo awiri onsewo adzakhala ogwirizana.+ Yohane 12:34 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 34 Pamenepo khamu la anthulo linamuyankha kuti: “Ife tinamva m’Chilamulo kuti Khristu adzakhala kosatha.+ Nanga inu mukunena bwanji kuti Mwana wa munthu adzakwezedwa m’mwamba?+ Kodi Mwana wa munthu ameneyo ndani?”+ Chivumbulutso 22:16 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 16 “‘Ine Yesu, ndinatumiza mngelo wanga kudzachitira umboni zinthu izi kwa inu, kuti zithandize mipingo. Ine ndine muzu+ ndi mbadwa+ ya Davide. Ndinenso nthanda yonyezimira.’”+
16 Nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhazikika pamaso pako mpaka kalekale. Mpando wako wachifumu udzakhazikika mpaka kalekale.”’”+
17 Dzina lake likhalebe mpaka kalekale.+Nthawi zonse pamene dzuwa latuluka, dzina lake lizitchuka,Ndipo kudzera mwa iye, anthu apeze madalitso.*+Mitundu yonse ya anthu imutche wodala.+
11 Nthambi+ idzatuluka pachitsa cha Jese,+ ndipo mphukira+ yotuluka pamizu yake idzakhala yobereka zipatso.+
5 “Taonani! Masiku adzafika,” watero Yehova, “ndipo Davide ndidzamuutsira mphukira yolungama.+ Ndithudi mfumu idzalamulira+ m’dzikoli ndi kuchita zinthu mozindikira, motsatira malamulo komanso mwachilungamo.+
13 Munthu ameneyu adzamanga kachisi wa Yehova ndipo adzalandira ulemerero.+ Iye azidzalamulira atakhala pampando wake wachifumu ndipo adzakhalanso wansembe ali pampando womwewo.+ Maudindo awiri onsewo adzakhala ogwirizana.+
34 Pamenepo khamu la anthulo linamuyankha kuti: “Ife tinamva m’Chilamulo kuti Khristu adzakhala kosatha.+ Nanga inu mukunena bwanji kuti Mwana wa munthu adzakwezedwa m’mwamba?+ Kodi Mwana wa munthu ameneyo ndani?”+
16 “‘Ine Yesu, ndinatumiza mngelo wanga kudzachitira umboni zinthu izi kwa inu, kuti zithandize mipingo. Ine ndine muzu+ ndi mbadwa+ ya Davide. Ndinenso nthanda yonyezimira.’”+