Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Genesis 1:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Motero Mulungu analenga zilombo zikuluzikulu za m’nyanja+ ndi chamoyo chilichonse chokhala mmenemo.+ Nyanja inatulutsa zimenezi zambirimbiri monga mwa mitundu yake.+ Analenganso chamoyo chilichonse chouluka monga mwa mtundu wake. Ndipo Mulungu anaona kuti zili bwino.

  • Salimo 74:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Inu munavundula nyanja ndi mphamvu zanu.+

      Pakati pa madzi munadula mitu ya zilombo za m’nyanja.+

  • Yesaya 51:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Dzuka! Dzuka! Vala mphamvu,+ iwe dzanja la Yehova!+ Dzuka ngati masiku akale, ngati m’mibadwo yakalekale.+ Kodi si iwe amene unaphwanyaphwanya Rahabi,+ amene unabaya* chilombo cha m’nyanja?+

  • Ezekieli 29:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Unene kuti, ‘Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Ine ndilanga iwe Farao mfumu ya Iguputo.+ Ndiwe chilombo chachikulu cha m’nyanja+ chimene chagona m’ngalande zake zotuluka mumtsinje wa Nailo.+ Ndiwe chilombo chimene chanena kuti, ‘Mtsinje wa Nailo ndi wanga, ndipo ineyo ndinaupanga ndekha.’+

  • Ezekieli 32:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 “Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yoimba polira yokhudza Farao, mfumu ya Iguputo. Uuze mfumuyo kuti, ‘Iwe wawonongedwa ngakhale kuti unali ngati mkango wamphamvu pakati pa mitundu ina ya anthu.+

      “‘Unali ngati chilombo cham’nyanja.+ Nthawi zonse unali kuyenda mwamphamvu ngati madzi m’mitsinje yako, ndipo unali kuvundula madzi ndi mapazi ako ndi kudetsa mitsinjeyo.’

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena