6 M’chaka cha 9 cha Hoshiya, mfumu ya Asuri inalanda Samariya+ n’kutenga Aisiraeli kupita nawo ku Asuri.+ Mfumuyo inakaika Aisiraeliwo ku Hala+ ndi ku Habori pafupi ndi mtsinje wa Gozani,+ ndiponso m’mizinda ya Amedi.+
14 Ine ndidzakhala ngati mkango wamphamvu kwa Efuraimu+ ndiponso ngati mkango wamphongo kwa nyumba ya Yuda. Ineyo ndidzawakhadzulakhadzula ndekha ndi kuwataya ndipo sipadzakhala wowalanditsa.+