Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mafumu 17:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Kenako mfumu ya Asuri inatenga anthu kuchokera ku Babulo,+ Kuta, Ava,+ Hamati,+ ndi Sefaravaimu+ n’kuwakhazika m’mizinda ya Samariya,+ m’malo mwa ana a Isiraeli. Anthuwo anatenga Samariya n’kumakhala m’mizinda yake.

  • Yesaya 10:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 “Yehova akadzatsiriza ntchito yake yonse m’phiri la Ziyoni ndi mu Yerusalemu, ndidzalanga mfumu ya Asuri chifukwa cha zipatso za mwano wa mumtima mwake ndiponso chifukwa cha kudzikuza kwa maso ake onyada.+

  • Yesaya 30:31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Chifukwa cha mawu a Yehova, dziko la Asuri lidzagwidwa ndi mantha,+ ndipo iye adzalimenya ndi ndodo.+

  • Nahumu 3:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 “Abusa ako ayamba kuwodzera,+ iwe mfumu ya Asuri, ndipo anthu ako olemekezeka akungokhala m’nyumba zawo.+ Anthu ako amwazikana pamapiri ndipo palibe amene akuwasonkhanitsa pamodzi.+

  • Zefaniya 2:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 “Iye adzatambasulira dzanja lake kumpoto ndipo adzawononga Asuri.+ Adzachititsa Nineve kukhala bwinja,+ kukhala dziko lopanda madzi ngati chipululu.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena